Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 323
Paphata pa Chichewa
Pepetula: Mawu amenewa amagwiritsidwa ntchito ponena
za zikhulupiriro zomwe anthu a ku Africa kuno amakhala
nazo zoti anthu amatha kulodzana kapena kuchitisa kuti
wina akumane ndi tsoka.
Chitsanzo: Sakumva masiku ano, akungokhala ngati
amupepetula.
Perekeza ndi maso: Kuyang’ana munthu moloza kumene
akulowera.
Chitsanzo: N’chifukwa chiyani amandiperekeza ndi maso?
Perekeza: Kutuma munthu komwe amakonda kupitako.
Chitsanzo: Iyeyu anaonako kadona kumeneko, ndiye ku-
mutumanso komweko n’kumuperekeza.
Peremende: Mwamuna wadazi lalikulu.
Chitsanzo: Mnyamata uyu ali ndi masweswe aakulu.
Akadzakula adzakhala peremende.
Petapeta: Kuweramawerama.
Chitsanzo: (1) Udzu unkangoti petapeta. (b) Akamayenda
amangoti petapeta.
Phala:
(a) Kuyankhula zopanda nzeru.
Chitsanzo: Mwayakhulazitu ndi phala lenileni.
(b) Chakudya choundana chamadzimadzi.
Chitsanzo: Andiphikira phala lampunga.
Phamula: Pakula zonse, tenga zonse.
Chitsanzo: Ndani waphamulamo ndiwo zija?
Phamuphamu: Zambirimbiri.
Chitsanzo: Akati akugawire amangokupatsa
phamuphamu.
Phava:
(a) Ndi dzina lotchulira zinthu zambiri monga nthochi.
Chitsanzo: Andipatsa phava limodzi la nthochi.
(b) Mvekero wa chinthu chomwe chagwera m’madzi.
322