Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 32
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: Achidyamakanda samalakwa, amalakwa ndi
anawa. Kususukira tchipisi.
Chidzadziwe n’chipande powomola: Aliyense
adzalandira mphoto yomuyenera.
Chitsanzo: Amene akuchita ulesi adzadya ulesi wawo
womwewo. Chidzadziwe n’chipande powomola.
Chidzam’mphepo: Munthu wofika mosayembekezereka
kapena wobwera asanaitanidwe.
Chitsanzo: Chitani changu, angatipeze chidzam’mphepo.
Chidzete: Munthu wopusa, chitsiru.
Chitsanzo: (1) Panopa mpamene ndazindikira kuti
munthu uja ndi chidzete. (2) Chimenechi ndi chidzete.
Chidzika: Kumangokhala osachitapo kanthu,
kudikiriritsa munthu wina.
Chitsanzo: Si bwino kumangochidzika mtsikana,
osamufunsira.
Chifunga:
(a) Nkhungu ya mitambo.
Chitsanzo: Kunjaku kwachita chifunga.
(b) Tiyi wosakwanira mkaka.
Chitsanzo: Anatipatsa tiyi wachifunga.
Chifwamba: Kubisalira ena kuti uwabere, umbanda.
Chitsanzo: Muthengo limeneli mukumabisala
achifwamba.
Chifwirimbiti:
(a) Kudutsa kwa nthawi.
Chitsanzo: Chifwirimbiti cha nthawi chikadutsa, nkhaniyi
iyiwalika.
31