Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 318
Paphata pa Chichewa
Pakamwa padzaulukira mbereswa: Udzapalamula.
Chitsanzo: Osamangoyankhulayankhula pakamwa
pangaulukire mbereswa.
Pakamwa papite mphepo: Kukhalako osadya.
Chitsanzo: Mwana ameneyu safuna kuti pakamwa pake
papite mphepo.
Pakamwa podya therere: Wonama.
Chitsanzo: Osamakhulupirira zimene amakuuzani,
pakamwa pake m’podya therere.
Pakamwa podya zamchere: Munthu ukhoza kulakwitsa
m’kayankhulidwe kapena kunena bodza.
Chitsanzo: Muzingotikhululukira, apa ndi pakamwa
podya zamchere.
Pakamwa:
(a) Munthu wodziwa kuyankhula
Chitsanzo: Amene uja ndi wochenjera pakamwa.
(b) Wolongolola.
Chitsanzo: Mwana uyu ndi wapakamwa.
Pakati: Kuyembekezera mwana.
Chitsanzo: Azimayi apakati amafunika kumapita ku-
chipatala nthawi zonse.
Pakhonde: Nthawi yolira maliro, achibale ndi ena apafupi
amapatsidwa malo oti agone ndipo nthawi zambiri
pamakhala pakhonde. Chifukwa cha zimenezi, pakhomo
anthu akapita kukagona kumaliro kaya agona m’nyumba,
amangoti adagona pakhonde.
Chitsanzo: Mfumu itamwalira, anthu adagona pakhonde
masiku awiri.
Pakhota mchira wanyani: Pamene pali vuto.
Chitsanzo: M’malo momangokangana, tiyeni tiyambe
taona kaye pakhota mchira wanyani.
317