Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 310

Paphata pa Chichewa Nyota: (a) Mawu achipongwe kwambiri onena za munthu amene akulira. Chitsanzo: Ndani akunyota kuseriyo? (b) Kabatani kaulemu komwe asilikali amalandira. Angatanthauzenso kupatsidwa ulemu. Chitsanzo: Mkulu uja walandiranso nyota ina. Nyowa: Kuchita manyazi aakulu. Chitsanzo: Mnyamata wochenjeretsa uja ananyoweratu atamugwira ataba 50 kwacha. Nyumba yaikulu: Kuchimbudzi. Chitsanzo: Akatuluka kunyumba yaikulu, mukawatsirire madzi osamba m’manja. Nyumba yodontha: Wolongolola kwambiri. Chitsanzo: Akazi awo aja ndi nyumba yodontha. Nyumwa: Kuioperera, kukaikira, kukana. Chitsanzo: Ndinainyumwa atandiuza akalandira ndalama sabweza. Nyung’unya: (a) Kuwawasa. Chitsanzo: Mandimuwa akunyung’unya. (b) Kukuvutitsa maganizo, kungofuna kukupweteketsa mtima. Chitsanzo: (1) Akumadutsa ndi kanjinga kawo kaja kuti atinyung’unyemo. (2) Sindingamufunsire, ndimangofuna kumunyung’unya. Nyungu kubalira kumphuno: Kuchitika potsiriza. Chitsanzo: Zaka zonsezi ndakhala ndikusowa zinthu zimenezi, ndiye n’kuzipeza pano ndithu! Nyungu yabalira kumphuno. Nzama m’kamwa nde: Kusowa mawu onena. Chitsanzo: Atamufunsa kuti anenepo maganizo ake, anangoti nzama m’kamwa nde! 309