Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 309
Paphata pa Chichewa
Nyenyeswa: Tiziduswa ta chakudya kapena zinthu zina.
Chitsanzo: Angondisiyira nyenyeswa za buledi.
Nyenyezi: Atsikana okongola.
Chitsanzo: Mnyamata wamfupi uja wagwira kanyenyezi
kapamtundapo.
Nyika:
(a) Kunama
Chitsanzo: Koma zimenezi n’zoona, sakutinyika ameneyu?
(b) Kuchita zosalongosoka, kuwononga zinthu.
Chitsanzo: (1) Ntchito ija angonyika. (2) Ndimaopa
kuyankhula kuopa kuti ndinganyike.
Nyimbo yafika patisowe: Yafika pakolasi.
Chitsanzo: Nyimboyo itafika patisowe, anthu anachita
kuwelama nayo dansi.
Nyinyirika: Kuchita zinthu mokakamizika, kusafuna
kuchita chinthu.
Chitsanzo: Mwanayu akumanyinyirika ndikamutuma.
Nyivula: Chita mwano, kupinda milomo moonetsa
mwano.
Chitsanzo: Anthu onse omwe anali pamwambowo
anayamba kunyivula, ataona kuti mfumuyo ikuyankhula
zopanda nzeru.
Nyodola: Nyoza.
Chitsanzo: Utangochoka muja anayamba kukunyodola.
Nyominyomi: Kuyenda mowerama, mwamantha kapena
mwaulemu. Angatanthauzenso kuyenda modzichepetsa.
Chitsanzo: Anyamata ena akaona mtsikana amangoti
nyominyomi pambuyo pake.
Nyontcholi (nyontchololo): Kunyowa.
Chitsanzo: Ndinawapeza ali nyontcholi.
Nyota yong’alula kukhosi: Ludzu.
Chitsanzo: Tigaireni madzi, nyota yang’alula kukhosi.
308