Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 307

Paphata pa Chichewa Nyambo: Kachakudya komwe anthu amaika pamsampha kapena pambedza kuti nyama kapena munthu akopeke. Mawuwa amakhala chining’a tikawagwiritsa ntchito potanthauza chinthu chimene chimaikidwa penapake kapena kuchitidwa kuti chikope wina. Chitsanzo: (1) Mayesero alionse amakhala ndi nyambo. (2) Sungaphe nsomba popanda nyambo. Nyamu: (a) Ngumbi. Chitsanzo: Lero tidyera nyamu. (b) Mvekero wosonyeza kunyamuka. Chitsanzo: Ataona kuti nyerere zawakwera anangoti nya- mu! Nyanga: (a) Zinthu zomwe zimakhala pamutu pa nyama. Chitsanzo: Mbuzi ili ndi nyanga ija yathyoka mwendo. (b) Zithumwa, nsupa. Chitsanzo: Munthu ameneyu amadalira nyanga. (c) Munthu wokhwima, mfiti. Chitsanzo: Munthu ameneyu ndi wanyanga. Nyangu: Manthongo oyera a m’maso. Chitsanzo: Sindifuna mwamuna wa nyangu. Nyani: Mawuwa amanenedwa akamanyoza munthu yemwe si wooneka bwino. Chitsanzo: Munyimbo ina mtsikana ankanyoza mnyamata pomuuza kuti, ‘Unali ndani iwe! Tinkadabwatu kuti kodi nyani ameneyu ndi wa ndani?’ Nyansi: Matudzi, bibi, manyi, matope, zinthu zoipa. Chitsanzo: Ndaponda nyansi. Nyansi: (a) Manyi, bibi. Chitsanzo: Nyansi zili kuserizo ndi za ndani? (b) Uve, zopanda ukhondo, zalitsiro. Chitsanzo: Kapuyitu ili ndi nyansi. 306