Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 305
Paphata pa Chichewa
Nthongo:
(a) Mbamu.
Chitsanzo: Uzitemba nthongo zogwirizana ndi msinkhu
wako!
(b) Zinthu zomwe zimatuluka m’mbali mwa maso.
Chitsanzo: Tamuchotsani manthongo mwanayo.
Nthongo: Mbamu.
Chitsanzo: Ndani wanditengera nthongo yanga?
Nthuku: Mtima wokwiya.
Chitsanzo: Atayamba kubweza moto, mtima wangawu
unachita nthuku ndipo ndinkafuna kumupanda.
Nthuli: Nyama yophikidwa yomwe ndi yoduladula.
Chitsanzo: Aliyense atenge nthuli imodzi.
Nthumanzi: Mantha.
Chitsanzo: Zimene achitazi zandichititsa nthumanzi.
Nthumbi: Kumwalira kwa mkazi pa nthawi yobereka,
maliro a mkazi wapakati.
Chitsanzo: (1) Mkazi wake anamwalira nthumbi. (2) Maliro
achitika pamtundapo ndi a nthumbi.
Nthumbidwa: Mwana wamng’ono amene pamutu pake
padaponda winanso wakhanda, kapena mwana wakhanda
pamene mayi wake ali ndi pakati.
Chitsanzo: Sabata yatha tinakazonda matenda. Imadwala
ndi nthumbidwa yawo ija.
Nthumwi: Munthu wotumidwa kukachita zinazake
kapena kukaimira munthu wina.
Chitsanzo: Atumiza nthumwi yawo.
Nthutumba: Chiwalo cham’mimba chomwe chimakhala
ndi nchenga mkati.
Chitsanzo: Ine ndidyera nthutumba.
Nthyamba: Munthu waulesi.
Chitsanzo: Ndani angasunge nthyamba pakhomo pake?
304