Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 304
Paphata pa Chichewa
Nthawi yachikuda: Nthawi yochedwa, kuchita zinthu
mochedwa, mosagwira nthawi.
Chitsanzo: Ife timayendera nthawi yachikuda.
Nthawi yochira: Nthawi yobereka mwana.
Chitsanzo: Ikakwana nthawi yochira pamafunika kuchita
zinthu mosamala.
Nthawi yoipa: Nthawi yosayenera kuchita zinthu, nthawi
ya mavuto.
Chitsanzo: Zinthu zimenezi zabwera pa nthawi yoipa.
Nthawi yotaika: Mochedwa, kuchedwa.
Chitsanzo: Anabwera nthawi yotaika.
Nthawi yowawitsa: Nthawi yovuta.
Chitsanzo: Tikukhala munthawi yowawitsa.
Nthawi yoyamba: Koyamba, ulendo woyamba.
Chitsanzo: Ino ndi nthawi yoyamba kukumana nawo.
Nthenda ya kumwezi: Khunyu.
Chitsanzo: Akazi awo aja amadwala nthenda ya kumwezi.
Ntheng’eneng’e: Kuchititsa mantha.
Chitsanzo: Munthu emeneyu amandipatsa
ntheng’eneng’e.
Ntheradi: Ndithudi. Mawuwa amanenewa potsindika kuti
zimene ukunena ndi zoona.
Chitsanzo: Ntheradi, anandiuza kuti akubwera!
Nthetemya: Mawu osalala, mawu abwino.
Chitsanzo: Akazi amakhala ndi mawu a mthetemya.
Nthiti:
(a) Mkazi.
Chitsanzi: Ndipite kumudzi ndikatenge nthiti yanga.
(b) Mafupa a pachifuwa.
Chitsanzo: Anachita ngozi moti wathyoka nthiti zitatu.
303