Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 299

Paphata pa Chichewa Nsalu ya lekaleka: Mwana wakhanda. Mawuwa amagwir- itsidwa ntchito chifukwa makolo ambiri salola kuti mwana wakhanda anyamulidwe ndi aliyense kuopera ku- mupweteka. Akaona wina akufuna kumunyamula ama- muuza kuti leka, usamugwire. Chitsanzo: (1) Banja la Achisale lagula nsalu ya lekaleka. (2) Mwamunayo wakwatiranso chifukwa akufuna nsalu ya lekaleka. Nsalu yasilika: Nsalu yotelera. Chitsanzo: Ndani wagula nsalu yasilikayi. Nsambi: (a) Kudziwa kusambira. Chitsanzo: Mwanayu amadziwa nsambi. (b) Mawuwa amanenedwa wina akakhala kuti walakwa. Chitsanzo: Nsambi, mungamutsine mwana choncho! Nsanamila: (a) Mtengo womwe amaimikira denga kuti lisagwe. Chitsanzo: Muzike nsanamila. (b) Munthu wodalilika. Chitsanzo: Bambowa ndi nsanamila ya pamudzi pano. Nsanamila: Munthu wodalilika. Chitsanzo: Bamboyu ndi nsanalila ya mpingowu. Nsanamirakande: Nkhumba. Chitsanzo: Bizinezi ya nsanamirakande ndi yotentha masiku ano. Nsangala: Waubwenzi. Chitsanzo: Alendo amafunika kuwalandira mwansangala. Nsangalatsi: Munthu amene amasangalatsa anthu monga wazisudzo kapena woimba. Chitsanzo: Anthu anabwera mwaunjinji kudzatsanzikana ndi nsangalatsi wawo. Nsangamutu: Mpango womwe anthu amamanga kumutu pamaliro kapena akamadwala. 298