Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 298
Paphata pa Chichewa
Nkuna: Nsapato.
Chitsanzo: Wavala kankuna kakuda.
Nkunkhuniza: Bodza lalikulu, kukokomeza.
Chitsanzo: Akunenalo ndi bodza la nkunkhuniza.
Nkwiyo wosaneneka: Kukwiya kwambiri.
Chitsanzo: Ndili ndi nkwiyo wosaneneka.
Nong’ona: Yankhula mwapansipansi.
Chitsanzo: N’chifukwa chiyani ukunong’ona?
Nong’oneza bondo: Kudandaula utapeza mavuto chifu-
kwa chosamva.
Chitsanzo: (1) Anyamata amene anasiya sukulu lero
akunong’oneza bondo. (2) Zimene mukuchitazi
mudzanong’oneza nazo bondo.
Nong’oneza nkhani: Mwina chifukwa cha mantha, anthu
ena anawuzana nkhani mwachinsinsi n’cholinga choch-
enjezana.
Chitsanzo: Tabwerani ndikunong’onezeni pang’ono.
Noninoni: Zokwanira bwino mafuta.
Chitsanzo: (1) Pamene amabwera kuphwandoko pakamwa
pake panali noninoni. (2) Ndiwo zake ndi zanoninoni.
Nsakanizo wakupha: Zinthu zoti sizingayendere limodzi.
Ngati zitayendera limodzi pakhoza kukhala mavuto aaku-
lu.
Chitsanzo: (1) Umene mukupanga apawu ndi nsakanizo
wakupha, zikhoza kukutsegulani m’mimba zimenezo. (2)
Umbuli ndi khama ndi nsakanizo wakupha.
Nsakanizo woopsa: Zinthu zoti sizingayendere limodzi.
Ngati zitayendera limodzi pakhoza kukhala mavuto aaku-
lu.
Chitsanzo: (1) Umene mukupanga apawu ndi nsakanizo
woospa, zikhoza kukutsegulani m’mimba zimenezo. (2)
Umbuli ndi khama ndi nsakanizo woopsa.
297