Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 297
Paphata pa Chichewa
(b) Chifunga, chizirezire.
Chitanzo: Kunjaku kwachita nkhungu.
Nkhunguni: Womana.
Chitsanzo: Abambo amenewa ndi nkhunguni, amachoka
pakhomo ngati alibe kalikonse, n’kupita kukamtini
kukagula tiyi ndi chikonda moyo chake.
Nkhuntha: Kupusa.
Chitsanzo: Nkhuntha imeneyi adzaichenjeretsa anzake.
Nkhutukumve: Munthu wosamva, wongotsata zake zo-
kha.
Chitsanzo: (1) Pasukulu pano sitifuna nkhutukumve. An-
thu okhawo amene abwerera sukulu ndi amene angakhale
pano! (2) Mwana uyu ndi nkhutukumve.
Nkhwangwa pamwala ga: Kukanitsitsa.
Chitsanzo: Atamupempha kuti apite anangoti nkhwangwa
pamwala ga!
Nkhwangwa yatema bondo: Zachitika pabanja pomwepo.
Chitsanzo: Mlandu wake ukhala wovuta kuweruza
chifukwa nkhwangwa yatema bondo.
Nkhwesa: Kusafuna kumva za anzawo kapena liuma.
Chitsanzo: Amuna awo anyanya nkhwesa.
Nkhwidzi: Mtima woipa, mtima womangofuna zonse
zikhale zako.
Chitsanzo: Akazi anu ndi ankhwidzi.
Nkhwirikwinya: Mbaala zomwe zimabwera chifukwa
chowotha moto.
Chitsanzo: Mkazi woyera safunika kumaotha moto poopa
nkhwirikwinya.
Nkhwiru: Wokonda kudya nyama, wosakonda masamba.
Chitsanzo: Mwanayu ndi wankhwiru.
Nkulukulu: Munthu wamkulu.
Chitsanzo: Zoona munthu nkulukulu angamayende
osavala mwado!
296