Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 296

Paphata pa Chichewa Nkhuku ya pamazira: Kupupuluma kapena kuvuta. Nkhuku ya pamazira imakhala yovuta kwambiri chifukwa imaona ngati munthu akufuna kutenga mazira ake. Chitsanzo: Saugwira mtima, amangokhala ngati nkhuku ya pamazira. Nkhuku yachikuda: Nkhuku yalokolo. Chitsanzo: Atiphikira nkhuku yachikuda. Nkhuku yachizungu: Nkhuku yahaibulidi. Chitsanzo: Sindidya nkhuku zachizungu. Nkhuku yoweta sagula pamsika: Mkazi sapeza moyenda. Mawuwa anabwera chifukwa nthawi zambiri nkhuku zimene amagulitsa pamsika zimakhala ndi vuto, zina zimakhala kuti zikudwala kapena zameza singano. Chitsanzo: Ndinawauza achimwene kuti nkhuku yoweta sagula pamsika. Nkhulang’ona: Munthu wolimba mtima. Chitsanzo: Kugwira ntchito ngati zimenezi kumafuna nkhulang’ona. Nkhuli (nkhwiru): Kususukira nyama, kukonda nyama osati masamba. Chitsanzo: Anawa ndi a nkhuli. Nkhumano: Kukumana, malo amene pakumana misewu, malo omwe anthu amakumana. Chitsanzo: (1) Lero kuli nkhumano. (2) Tikakumane pa nkhumano. Nkhumbzi: Munthu wakuba. Chitsanzo: (1) Chenjerani naye ameneyu akuyeretsani m’maso. Ndi nkhumbzi. (2) Mukusungira nkhumbzi pakho- mo panu pano. Nkhungu: (a) Munthu wopusa kapena kuti wopepera. Chitsanzo: Nthawi zambiri munthu amene amaseka choncho amakhala nkhungu. 295