Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 295
Paphata pa Chichewa
Nkhomaliro: Chakudya chamasana.
Chitsanzo: Tiyeni tikachite nkhomaliro.
Nkhondo ndi anansi: Mawuwa amatanthauza kuti anza-
ko ndi amene amakuchitira chipongwe nthawi zina.
Chitsanzo: Andiukira ndithu ngati sakundidziwa, nkhondo
ndi anansi ndithu.
Nkhongo gwa! Mawu achipongwe onena za munthu
wopanda mnzeru kapena wosamva.
Chitsanzo: Tachioneni, chili nkhongo gwa, chikupitabe
komweko ngakhale kuti dzulo anachiphovomora.
Nkhono: Mawuwa amanena za munthu amene amachita
zinthu mochedwa kwambiri ngati mmene imachitira
nkhono.
Chitsanzo: N’chifukwa chiyani mwatuma nkhono ija.
Nkhonya (nkhonyo):
(a) Kumenya munthu ndi kuseri kwa chibakera chokunga,
kapena zala zopinda.
Chitsanzo: Anamukhoma nkhonya n’kumufunsa kuti,
“Lota, wakumenya ndani?”
(b) Masewera omenyana ndi zibakera.
Chitsanzo: Katswiri wina wochita masewera a nkhonya
anauza mnzake kuti akamabwera kudzamenyana naye
atengeretu bokosi lake.
Nkhonya yobwezera kuwawa: Mnzako akamakubwezera
zimene unamuchitira umamva kupweteka kwambiri.
Chitsanzo: Unandichitansotu zomwezi, kungoti khonya
yobwezera imawawa!
Nkhope itatembenuka: Nkhope itasintha.
Chitsanzo: Ndinawapeza nkhope itatembenuka.
Nkhope yachikoka: Nkhope yokongola.
Chitsanzo: Mwanayu ali ndi nkhope yachikoka.
294