Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 294
Paphata pa Chichewa
Nkhalwe: Nkhanza.
Chitsanzo: Bambowa ndi ankhalwe, amamenya akazi awo.
Nkhandwe: Munthu wachinyengo, wokonda kuchen-
jeretsa anzake.
Chitsanzo: Sindimadziwa kuti mwamuna wake uja ndi
nkhandwe.
Nkhani ndi kamnyamata: Nkhani sichepa.
Chitsanzo: Mukuti chiyani? Pajatu nkhani ndi kamnyama-
ta!
Nkhani yagona pati: Kodi vuto lili pati?
Chitsanzo: Mpofunika tidziwe kuti kodi nkhani yagona
pati.
Nkhani yochititsa nyansi: Nkhani yosakondweretsa,
yonyansa.
Chitsanzo: Ndangomva nkhani yochititsa nyansi.
Nkhani yodetsa kukhosi: Nkhani yosakondweretsa, yo-
detsa nkhawa.
Chitsanzo: Ndangomva nkhani yodetsa kukhosi.
Nkhata:
(a) Maluwa omwe anthu amaika pamanda.
Chitsanzo: Amagulitsa nkhata za maliro.
(b) Chinthu chimene munthu amaika pamutu kuti
chimene wasenza chisamamugogode.
Chitsanzo: N’chifukwa chiyani wasenza popanda nkhata?
Nkhatayagwa: Munthu wosakonda ntchito.
Chitsanzo: Mtsikana ameneyu ndi nkhatayagwa. Safuna
kugwira ntchito koma kudya basi.
Nkhatheya: Munthu waluso pa ntchito yake, munthu
wolemekezeka.
Chitsanzo: Kwabwera mikhatheya ya zomangamanga.
Nkholokolo: Munthu woyambanitsa anthu.
Chitsanzo: Anthu sati ayambana liti pamudzi pamene
paja. Ndikuganiza kuti pali nkholokolo.
293