Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 293
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: (1) Sindimadziwa kuti ndikuthawa njokaluzi.
(2) Sangakumenyeni, iwowaja ndi njokaluzi.
Njole: Mkazi wokongola
Chitsanzo: Nawenso upeze kanjole kako.
Njombwa: Ndalama.
Chitsanzo: Mwanayu wangochepa, koma amapeza njomb-
wa.
Njonda: Bambo.
Chitsanzo: Njonda inayake imafuna kumugwiririra.
Njovu: Munthu wonenepa kwambiri.
Chitsanzo: Mayi awo ndi njovu.
Nkadza apo ndaima: Mawu amene anthu amakonda
kunena akakhala kuti akumaliza kuyankhula makamaka
pamlandu.
Chitsanzo: Basitu, tsiku lina ndinangoona abweranso,
ndiye ine ndikanatani? Basi ndinangowalandira. Nkadza
apo ndaima!
Nkhakamila: Munthu wokakamira.
Chitsanzo: Mwana ameneyu ndi nkhakamira.
Nkhalamba yogwa n’kumina: Nkhalamba yotheratu,
munthu wokalamba kwambiri.
Chitsanzo: Pamudzi apa pali nkhalamba zogwa n’kumina.
Nkhalamo: Wankhanza.
Chitsanzo: Mayi amenewa ndi nkhalamo, amazunza ana a
anzawo.
Nkhali yadooka (nkhali yabooka): Mkazi wam’fera, akazi
awo amwalira.
Chitsanzo: Bambo amenewa nkhali yawo inadooka.
Nkhali: Mkazi.
Chitsanzo: Ndikufuna udzakhale nkhali yanga!
292