Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 292

Paphata pa Chichewa Nje: Kulibe, sizitheka. Chitsanzo: “Kodi munthu uja wabwera?” “Nje!” Njenjenje (kunjenjemera): Kugwedezeka chifukwa cha mantha kapena matenda. Chitsanzo: Ndinawapeza ali njenjenje. Njenjete: Munthu wadyera. Mawuwa anachokera ku ka- chilombo komwe kamadya zovala. Chitsanzo: (1) Njenjete zamudyera zovala. (2) Mwanayu ndi njenjete. Njerengo: Nkhani zongopeka. Chitsanzo: Amakonda kukamba njerengo. Njirayachepa: Wamatekenya, wopotoka mapazi. Chitsanzo: (1) Kukubwera njirayachepa. (2) Njirayachepa uja ali kuti? Njodo: Mimba yaikulu, yangati kamtsuko. Chitsanzo: Ambiri omwe amamwa wamasese amakhala ndi njodo. Njoka muudzu: Mawuwa amanena za munthu wachiny- engo komanso woipa amene amakonzera anzake chiwem- bu. Chitsanzo: Ali ngati njoka muudzu, podutsana amandim- wetulira koma mumtima muli tho dzimilandu. Njoka: (a) Munthu woipa. Chitsanzo: Pamene miyezi iwiri inkatha, mpamene ndina- zindikira kuti mkazi uja ndi njoka. (b) Munthu wosakonda kumwa madzi. Chitsanzo: Mwana ameneyu ndi njoka. Njokaluzi: Munthu wopanda mphamvu. Njokaluzi ndi chikopa chimene chimatsala, njoka ikufundula. Nthawi zi- na anthu amatha kuthawa chinthu chimenecho poganiza kuti ndi njoka yeniyeni. 291