Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 291

Paphata pa Chichewa Ngolowera: Kuwirira chifukwa cha udzu kapena chimanga. Chitsanzo: Musiye kudutsa njira zachidule, kunjaku kwachita ngolowera. Ngongole: Kubwereka ndalama kapena zinthu zamwini. Chitsanzo: Ngongole imakoma potenga koma pobweza imawawa. Ngozi: Maliro. Chitsanzo: Tathokoza kwambiri chifukwa choti mwatilondola mutamva za ngozi yatigwerayi. Nguli: Ndi kamtengo komwe kamakhala kosongoka mbali imodzi. Kamtengoka amakagwiritsa ntchito pochita masewera. Amakakwapula ndi lamba ndipo kamazunguli- ra. Chitsanzo: Akungozungulira ngati nguli. Nguwi (nkhufi): Chakudya chikakhalitsa chimamera nguwi, nthawi zinanso zovala zomwe zili pachinyezi zimamera nguwi. Chitsanzo: Nsima ya dzana ija yapanga nguwi. Ngwazi: Munthu wamphamvu, wotchuka, katswiri. Chitsanzo: Mwamuna ameneyi ndi ngwazi pankhondo. Nimurode: Munthu woipa kwambiri. Baibulo limatchula za munthu ameneyu kuti ndi amene anali woyambirira kukhala ndi mphamvu zambiri padzikoli komanso anali wankhanza kwambiri. Chitsanzo: Wapita kuti Nimurodi uja? Ninkha nyenwa: Kulonjeza chifukwa chofuna kutsan- galatsa ena. Chitsanzo: Andale a masiku ano akumangotininkha nyen- wa. Njala inatipha: Njala inatipweteka kwambiri. Chitsanzo: Tinakhala tsiku lonse osadya moti njala inatipha! 290