Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 290

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: (1) Zoonadi, ng’oma yolira kwambiri sichedya kusweka. Taonani wasiya ana amayereyere. (2) Mnyamata amene uja ndi ng’oma pankhani ya zisudzo. Ng’oo! Mawu omwe amanenedwa munthu wina akamauza mnzake kuti walephera, wauponda. Chitsanzo: Ngati umaganiza kuti uipeza itapsa, ng’oo! Ng’ung’udza: Yankhula mwapansipansi, kuchita mwano. Chitsanzo: (1) Ndani akung’ungudza kuseriko? (2) Mwana uyu amang’ung’udza ukamamutuma. Ngala: Maso a tirigu. Chitsanzo: Osamapulula ngala za tiligu zisanakhwime. Ngamila: Munthu wosakonda kumwa madzi, koma akati amwe amawamwa kwambiri. Chitsanzo: Bambo anu ndi ngamila. Nganga: (a) Munthu wokalamba, nkhalakale. Chitsanzo: (1) Kodi anganga aja apita kuti? (2) Nganga zonse zinatha kumwalira. (b) Chidale, chifuwa. Chitsanzo: Mpirawo anauika panganga. Nganganga: Osafuna kusiya kapena kusintha. Chitsanzo: Nthawi zonse amangoti nganganga pa zimene akudziwa, safuna kusintha maganizo. Ngaphwete: Makonda kuseka. Chitsanzo: Anawa ngaphwete. Ngenge (dzuwa zii): Mtsikana wokongola kwambiri. Chitsanzo: (1) Ndagwira kangenge kenakake. (2) Ku- kubwera dzuwa zii. Ngodya: Pakona. Chitsanzo: Mwala umene amisiri anaukana unasanduka wapangodya. 289