Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Seite 29
Paphata pa Chichewa
Chibaluwa: Kalata.
Chitsanzo: Ndikuganiza zowalembera chibaluwa.
Chibenga: Chitsiru. Mawu amenewa amagwira ntchito
tikamanena za munthu yemwe ndi wopanda nzeru
mpang’ono pomwe.
Chitsanzo: Achimwene anu aja ndi chibenga.
Chibengere: Chitsiru
Chitsanzo: Kumalemekeza zibengere kuti upewe phokoso.
Chiboli: Chilombo chomwe chimaoneka mowala chifukwa
chilibe ubweya. Anthu amanena mawuwa ponena za
munthu amene wametetsa mpala.
Chitsanzo: Kodi ziboli zija zadutsa apa?
Chiboliboli: Munthu wopanda nzeru yemwe akakhala
pagulu amangokhala duu. Tanthauzo lake lenileni ndi
chinthu chosema pofanizira chinachake.
Chitsanzo: Chapita kuti chiboliboli chija?
Chibufumpweya: Chinthu chopanda kanthu, chiphwafu.
Chitsanzo: Banzi limene anandipatsa linali
chibufumpweya.
Chibwana cha nchombo lendee: Chibwana chachikulu.
Chitsanzo: Chimene akuchitachi ndi chibwana cha
nchombo lendee!
Chibwana chimatuma: Mawuwa amanenedwa ngati
munthu wachita zinthu chifukwa chosaganiza bwino
kenako n’kumadandaula.
Chitsanzo: Sindinakuuzeni kuti chibwana chimatuma?
28