Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 287

Paphata pa Chichewa pakhomo pano! Ndikupanga masamu: Ndikuganiza zochita. Chitsanzo: Ndikupanga masamu a mmene ndingapezere ndalama zogulira foni imeneyi. Ndilekere? Chondiletsa n’chiyani? Chitsanzo: “Upita kudansi?” “Ndirekere?” Ndilibe nawo mawu: Amandisowetsa chonena. Chitsanzo: Ana anuwa ndilibe nawo mawu. Ndilije: Mawu okokomeza ponena kuti ulibe. Chitsanzo: Ine vuto ndilije, ali nalo ndi amene aku- werewetawo. Ndimangokuyang’anani: Ndimangokusiyani, ndimadziwa kuti mukumana nazo. Chitsanzo: Inetu ndimangokuyang’anani, ndimadziwa kuti zikavuta mubwera. Ndimbwandimbwa: Kamvekedwe ka kufewa kwa chinthu. Chitsanzo: Matilesiwo amangoti ndimbwandimbwa. Ndimuthira dothi m’khutu: Ndikupha. Chitsanzo: Akachita masewera ndimuthira dothi m’khutu. Ndindindi: Anthu ambiri, kuwirira. Chitsanzo: (1) Pakhomo pawo mitengo inangoti ndindindi. (2) Ndinapeza anthu ali ndindindi pakhomopo. Ndipsi: Munthu wochita zoipa zosadziwika kwa anthu. Chitsanzo: Musawaone kutchena kuja, iwowajatu ndi ndipsi. Ndithane nazo: Kungochita kuti umalize basi. Chitsanzo: Ndimangochita kuti ndithane nazo. Ndiweyani: Waukulu. Chitsanzo: Kunjaku kuli mdima wa ndiweyani. Ndodomtolo: Osadziwa chochita kapena chonena. Chitsanzo: Nditamva zimene amanena, ndinangoti ndodomtolo. 286