Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 286

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: (1) Madzi a mutsukowo amangoti ndengundengu. (2) Ndimachita mantha bwato likayamba kuchita ndengundengu. Ndevu za ponya mtedza upaone: Ndevu zochuluka zedi zodzadza pachibwano komanso m’masaya. Chitsanzo: Bambo ake ali ndi ndevu za ponya mtedza upaone. Ndevu zampanda: Ndevu zochuluka zedi zodzadza pa- chibwano komanso m’masaya. Chitsanzo: Bambo ake ali ndi ndevu zampanda. Ndewu ya phwee: Ndewu yoopsa. Chitsanzo: Mtchalitchi mukumachitikanso ndewu ya phwee! Ndewu yafumbi: ndewu yoopsa. Chitsanzo: Kumsikaku kunali ndewu yafumbi. Ndewu yamtima bii: Ndewu yoopsa. Chitsanzo: Kutchalitchiku kunali chindewu chamtima bii. Ndi mwalamwala: Ndi wolimba, wodalilika, wamphamvu. Chitsanzo: (1) Mwana ameneyu ndi mwalamwala, sangaledzere ndi kapu imodzi. (2) Agogowa ndi mwalamwala, amalima ngati adakali mnyamata. Ndi patali: Waluso kwambiri. Chitsanzo: Amene uja ndi patali, sungamupose kutha- manga. Ndi ulendo: Mawuwa amanenedwa potamanda munthu yemwe amachita zinazake mwaluso. Kunena kwina timati “si masewera.” Chitsanzo: Mwana uyuyu ndi ulendo! Ndi wautali: Kuyenda ulendo wautali. Chitsanzo: Ndikangomaliza kugwira ntchito, ndi waulali. Ndigwira mtengo wanji: Nditani ine? Chitsanzo: Ndigwira mtengo wanji mukandithamangitsa 285