Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 285
Paphata pa Chichewa
Ndanenandanena: Wosamva za ena.
Chitsanzo: Bwana amene aja ndi ndanenandanena.
Ndangodutsamo sindinatchole nkhwani: Ndangonena,
sindinapalamule mlandu.
Chitsanzo: Kodi mukuwanena achimwene anu eti? Ayi,
inetu ndangodutsamo sindinatchole nkhwani.
Ndapota nanu: Pepani, ndikukupemphani.
Chitsanzo: Ndapota nanu, ndikhululukireni.
Ndapotananu: Kuchonderera.
Chitsanzo: Ndapotananu, ndikhululukireni.
Ndauyambatu: Mawuwa amanenedwa munthu akaman-
yamuka pamalo.
Chitsanzo: Ndauyambatu, mundipeza!
Ndawachita zinthu: Ndawalanga.
Chitanzo: Ana amwano aja ndawachita zinthu.
Ndazitayira kudzala: Ndakhululuka.
Chitsanzo: Zonse zomwe anandichitira ndazitayira kud-
zala.
Ndaziyesa dzala: Ndakhululuka.
Chitsanzo: Zonse zomwe anandichitira ndaziyesa dzala.
Ndege: Botolo lothandiza anthu kudziwa kuti mowa
wapsa (makamaka kachaso).
Chitsanzo: Wapsa kumtundaku. Ndaonera ndege
pansewupo.
Ndekesha: Chikabudula chachikulu, chithewera.
Chitsanzo: Akamalima amavala ndekesha.
Ndendende: Kuchitika momwemo, osatsala chilichonse.
Chitsanzo: Ulosiwo unakwaniritsidwa ndendende.
Ndengundengu: Kugwedezeka kwa madzi kapena zinthu
zamadzimadzi, kugwedezeka kwa chinthu chomwe chili
pamadzi.
284