Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 284
Paphata pa Chichewa
Ndadya njinga: Mawuwa amanenedwa zikakhala kuti
munthu akunenetsa kuti sangachite zimenezo. M’mawu
ena angatanthauze kuti n’zosatheka.
Chitsanzo: Sindigayerekeze kugulitsa nyumba yanga
pokhapokha nditadya njinga.
Ndaimika manja: Ndalephera, kugonja.
Chitsanzo: Mwamuna ameneyu ayi, ndaimika manja.
Ndakhutakale: Munthu wachimimba chachikulu.
Chitsanzo: Amageya anyezi ambiri amakhala a
ndakhutakale.
Ndakhutandalema: Mpando wopangidwa moti munthu
amakhala ngati wagona. Nthawi zambiri umapangidwa
ndi matabwa ndipo pokhalira amaikapo chisaka kapena
nsalu.
Chitsanzo: Agogo akhala pampando wa ndakhutandalema.
Ndakoka: Ovololo.
Chitsanzo: Upemphe abwana ako akugulire ndakoka.
Ndakoka: Ovololo.
Chitsanzo: Wavala ndakoka.
Ndakupukwani: Ndakusowani.
Chitsanzo: Ndakupukwani amama.
Ndale:
(a) Kukola munthu wina kuti agwe.
Chitsanzo: Amakonda kutcherana ndale.
(b) Zimene anthu amachita poyendetsa dziko.
Chitsanzo: Ambiri amayamba ndale chifukwa cha dyera.
Ndamuopera: Wandichititsa mantha.
Chitsanzo: Ndamuopera, ndi munthu woipa kwambiri.
Ndandanda: Zinthu zolembedwa mwadongosolo.
Chitsanzo: Talembani ndandanda ya zinthu zimene
mukufuna.
283