Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 283
Paphata pa Chichewa
ataspa, m’modzi anadya pomwe wina sanadye. Winayo
anapusitsa mnzakeyo ngati nayenso adya nawo.
Chitsanzo: Ndinadziwa ine kuti akunamizana kudya galu.
Namondwe: Mphepo yaikulu ya panyanja. Mawuwa
angatanthauzenso mavuto.
Chitsanzo: Chaka chatha tinakumana ndi namondwe.
Namwali:
(a) Mkazi yemwe sanakwatiwe, mtsikana.
Chitsanzo: Kunyumba kwa Abengo kuli kanamwali.
(b) Munthu amene akuvinidwa, kulowa chinamwali.
Chitsanzo: Pakhomo pawo pachoka anamwali atatu.
Namwalikande: Nkhumba.
Chitsanzo: Atazindikira kuti timadya namwalikande,
anasiya kubwera kudzabwereka mapoto.
Namwino: Nesi.
Chitsanzo: Anamwino akuthawa m’dziko muno chifukwa
cha kuchepa kwa malipiro.
Namwino: Nesi.
Chitsanzo: Boma lalemba anamwino ambiri.
Nankungwi: Wolangiza mwana kuti akule bwino. Nthawi
zambiri amalangiza mwanayo pachinamwali.
Chitsanzo: Mayiwa ndi amene akhale nankungwi wa mwa-
nayu pachinamwalipa.
Napweri: Munthu woyera kwambiri nthawi zina ndi tsitsi
lomwe, alubino.
Chitsanzo: Aliyense wotchula alubino kuti napweri
azimangidwa.
Nchochombe: Munthu waluso kwambiri.
Chitsanzo: Imeneyi ndi michochombe yamasamu.
Ndachimina: Ndalapa, sindidzabwerezanso.
Chitsanzo: Ndachimina, sindidzadzeranso njira imeneyi.
282