Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 282
Paphata pa Chichewa
N’chake: Adazolowera.
Chitsanzo: Mtsikana amene uja m’chake, sadzasiya kuth-
amanga.
N’dzasamban’kadzafa: Nkhumba.
Chitsanzo: Akufuna ndikawakonzere n’dzasam-
ban’kadzafa.
N’dzayeran’kadzafa: Nkhumba.
Chitsanzo: Akufuna ndikawakonzere n’dzayeran’kadzafa.
N’zosachita kufunsa: N’zachionekere, n’zachidziwikire.
Chitsanzo: N’zosachita kufunsa kuti nafenso itikhudza
njalayi.
Nakubala: Munthu yemwe anabereka mwana.
Chitsanzo: Mpofunika kumalemekeza anakubala.
Namageyaanyezi: Munthu wolemera, wachuma.
Chitsanzo: Anamageyaanyezi samangira lamba, koma
taye.
Namageyaanyezi: Munthu wolemera.
Chitsanzo: Kukhala namageyaanyezi kulinso ndi kuipa
kwake, umasowa tulo.
Namandwa: Katswiri.
Chitsanzo: (1) Amenewa ndiye anamandwa a pakampani
pano. (2) Ameneyu ndi namandwa pankhani yokonza zi-
gayo.
Namanyonyolo: Katswiri.
Chitsanzo: Ameneyu ndi namanyonyolo pankhani zoimba-
imbazi.
Namfedwa: Munthu amene wachibale wake wamwalira.
Chitsanzo: Anamfedwa onse anauzidwa kuti asayambe
kulira mpaka amfumu atadziwitsidwa.
Namizana kudya galu: Kuikana m’mavuto, kunamizana.
Anthu awiri anauzana kuti aphe galu n’kumudya, koma
281