Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 280
Paphata pa Chichewa
Mwaza ndalama: Kuwononga ndalama.
Chitsanzo: Ndinkadziwa kuti akapitirizabe kumwaza
ndalama, adzasauka.
Mwazirana Makala: Vutana.
Chitsanzo: Pamudzi pajatu anthu amwazirana makala.
Mwemwetela: Kuonetsa nkhope yachisangalalo.
Chitsanzo: Ukumwemwetera chiyani?
Mweta: Tenga zonse.
Chitsanzo: Pamene ndimafika ndapeza atamwetapo
katundu yense.
Mwetera pansi: Kuchita mochenjera kwambiri.
Chitsanzo: Atambwali ambiri amakonda kumwetera pansi.
Mwezi udam’fera: Ali ndi pakati pa mwezi umodzi.
Chitsanzo: Mkazi wake mwezi udam’fera.
Mwezi wadza ndi thumba: Zodabwitsa.
Chitsanzo: Sitikudziwa kuti chichitike n’chiyani, mwezi
wadza ndi thumba.
Mwinifilimu safa: Mawuwa anayamba potengera zimene
zimachitika m’mafilimu kuti munthu yemwe ndi mwinifili-
mu samafa nthawi zambiri.
Chitsanzo: Zandivuta inde, koma mwinifilimu safa, zidza-
yenda.
Akita safa: Mawuwa anayamba potengera zimene zim-
achitika m’mafilimu kuti munthu yemwe ndi mwinifilimu
samafa nthawi zambiri.
Chitsanzo: Zandivuta inde, koma akita safa, zidzayenda.
Mwinjiro: Mkanjo.
Chitsanzo: Anthu a mayiko ena amavala mwinjiro.
Myendanazo: Munthu wamiseche, munthu woyenda ndi
mabodza.
Chitsanzo: (1) Udzasiya kumangouza anthu nkhani
ukadzakumana ndi myendanazo. (2) Myendanazo satha
phazi pakhomo la ena.
279