Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 279
Paphata pa Chichewa
Mwanditaya: Mwandisiya, simunandilemekeze,
mwandinyoza.
Chitsanzo: (1) Mwanditaya chifukwa ndilibe ndalama. (2)
Mukadzasauka adzakutayani.
Mwano: Kukana kuchita zinazake, chipongwe.
Chitsanzo: Mwanayu ndi wamwano.
Mwanzaneno: Ali wosavala.
Chitsanzo: Wamisalayo amangoyenda mwanzaneno.
Mwapatalipatali: Kunena mongosankha, kuchita zinthu
mongosankha.
Chitsanzo: Ndangowauza nkhani ija mwapatalipatali.
Mwatchutchutchu: Kuyankhula mosabisa mawu.
Chitsanzo: Munthuyu amangoyankhula mwatchutchutchu.
Mwatulukamotu m’botolomo! Mawuwa amanenedwa
munthu akakhala kuti wadzola mafuta ambiri.
Chitsanzo: Koma ndiye mwatulukamotu m’botolomo!
Mwaunyinji: Mawuwa amanenedwa ngati anthu ambiri
achita zinthu mogwirizana.
Chitsanzo: Anthu anabwera mwaunjinji kudzatsanzikana
ndi nsangalatsi wawo.
Mwauponda: Zakuvutani, mwalephera.
Chitsanzo: Ngati mumaganiza kuti mudutsa moyera,
mwauponda.
Mwaye: Utsi wokakamira kudenga m’khitchini kapena
m’nyumba.
Chitsanzo: Anthu ena amakhulupirira kuti mwaye ndi
mankhwala a m’mimba.
Mwayi wanzama: Mwayi waukulu.
Chitsanzo: Anzanu apeza mwayi wanzama wofukula ndi
manja.
Mwaza maso: Kuyang’ana uku ndi uku.
Chitsanzo: Ndinamwaza maso koma sindinaone chili-
chonse.
278