Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 278
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: (1) Ali ndi mwana wapatchire. (2) Amene ana-
berekera limodzi ndi awiri aja, wina uja ndi wapatchire
(wapathengo).
Mwana wopanda bambo ake: Mwana yemwe wabadwa
koma bambo ake sakudziwika. Nthawi zambiri amadziwa
ndi maya ake okhawo.
Chitsanzo: Ali ndi mwana wopanda bambo.
Mwana: Munthu wamkulu koma wosaganiza bwinobwino.
Chitsanzo: Bambo ameneyu ndi mwana.
Mwanaalirenji: Kusasowa kalikonse, kukhala ndi chili-
chonse.
Chitsanzo: (1) Pakhomo pakakhala pa mwanaalilenji, ana
samanyentchera kapena kutupikana. (2) Pakhomo pawo
ndi pa mwana alirenji.
Mwanamphepo: Matenda otuluka zilonda zomwe zim-
apsa.
Chitsanzo: Ameneyu ndi mwanamphepo.
Mwandichinya: Mawuwa amenedwa ndi munthu
potanthauza kuti munthu wina wamuposa.
Chitsanzo: Apatu ndiye mwandichinya, ndalephera
kupeza yankho lake.
Mwandipinda: Mawu amene munthu amayankhula
akakhala kuti sanamvetse zimene wina akunena, kapena
ngati wapusitsidwa ndi mnzake.
Chitsanzo: (1) Mwandipindatu pamenepa, mukutanthauza
chiyani? (2) Ndinakapeza yankho lake, kungoti
anandipinda.
Mwandisiya m’malere: Simunafotokoze zondikhutiritsa,
simunamalize.
Chitsanzo: Basi mwamaliza? Apa ndiye mwandisiya
m’malere!
277