Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 273

Paphata pa Chichewa Munatha inu: Zinkakuyenderani kale. Chitsanzo: Munatha inu, asiyeni anzanu ayendetse zinthu. Mundifwenthe: Mulote, mudziwe zimene ndikufuna kuchita. Chitsanzo: Ngati mukufuna kundidziwa, mundifwenthe. Mundilinge (mlingo): Mundiyeze, ngati kwa atelala. Chitsanzo: Atelala mundilinge ndi maso, amunanga nsanje! Mungondimaliza: Mungondipha. Chitsanzo: Mwandilanda munda, ndiye mukufunanso chi- yani, bwanji osangondimaliza? Munthu wadiso pamtunda: Wotengeka. Chitsanzo: Tauni ino sifuna munthu wa diso pamtunda. Munthu wamba: Munthu wosatchuka, wopanda udindo uliwonse. Chitsanzo: (1) Anakana kundithandiza chifukwa ndine munthu wamba. (2) Salola anthu wamba kulowa malo amenewo. Munthu waphula: Wopusa. Chitsanzo: Munthu amene ndinayenda nayeyo ndi waphula. Munthu wazala zazitali: Wakuba. Chitsanzo: M’tauni mwachuluka anthu a zala zazitali. Munthu wofaifa: Munthu wopanda mphamvu. Chitsanzo: Ntchito zotere sizifuna munthu wofaifa. Munthu wolemberera pamudzi: Wobwera kawirikawiri. Chitsanzo: Kodi mwana uyu akulembereranji pamudzi pano? Munthu wotsika: Munthu wamba, munthu wosauka. Chitsanzo: Safuna kudzakwatira ndi munthu wotsika. 272