Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 271

Paphata pa Chichewa Mtimwazire: Munthu woyambitsa mapokoso. Chitsanzo: Pamudzi pano panali bwino pasanafike mtimwazire uja. Mtokoma: Makalata oyenera kutengedwa n’kupititsidwa kwinakwake. Chitsanzo: Kwabwera mtokoma wanu. Mtsala: Zinthu zoti zanenedwa kale. Chitsanzo: Zimene mukunenazitu ndi mtsala. Mtsamiro: (a) Munthu wofa naye. Chitsanzo: Mukufuna mupite ndi mtsamiro? (b) Pilo. Chitsanzo: Tulo timakoma ukayedzeka mutu pamtsamiro. Mtsikana woyendayenda: Hule, mtsikana wokonda amu- na. Chitsanzo: Mtsikanayu ndi woyendayenda. Mtsinje umalimba ndi miyala: Ukadya mpamene umapeza mphamvu zoti ukhoza kugwira ntchito. Chitsanzo: Tiyeni tikadye amwene, mtsinje umalimba ndi miyala. Mtsukuluziro: Chimanga chomwe amaika muntchini akamaliza kugaya mphale kuti atsimikize kuti yonse yagayidwa. Chitsanzo: Mukamapita kukagayitsa mphaleyi musaiwale kutenga mtsukuluziro. Mtswatswa: Phokoso lomwe limamveka munthu ak- amaponda masamba ouma, kapena phokoso la mapazi a munthu akamayenda. Chitsanzo: Ndinadziwira mtswatswa kuti ndi achimwene. Mtudzu: Mwano. Chitsanzo: Sindifuna munthu wamtudzu pakhomo pano. 270