Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 270
Paphata pa Chichewa
Mtima wa mtengo: Pakati pa mtengo uliwonse
pamakhala polimba kwambiri. Pamenepo pamatchedwa
mtima wa mtengo.
Chitsanzo: Mtima wa mtengo umakhala wolimba kwambiri
moti sungadyedwe ndi chiswe.
Mtima wachiwala: Mtima woipa. Mawuwa anabwera ku-
chokera ku chiwala. Ukazula mutu wa chiwala,
chinachake chakuda komanso chonyansa chimasololoka
kuchokera mkati. Amatanthauza munthu amene ama-
kusekerera koma akukufunira zoipa mumtima.
Chitsanzo: Amakumwetulira pamaso koma ali ndi mtima
wa chiwala.
Mtima wadwale: Munthu woti sangasinthe, mtima woipa.
Chitsanzo: Simungamusinthe amene uja, ali ndi mtima
wadwale.
Mtima walasa phaso: Kukumbukira kumudzi kapena
chinthu china chofunika kwambiri.
Chitsanzo: Mpofunika ndibwerere kumudzi, mtima walasa
phaso!
Mtima wapachala: Munthu wopsa mtima msanga.
Chitsanzo: (1) Alitu ndi mtima wapachala. (2) Anthu a mti-
ma wapachala amakwatira akazi ofatsa.
Mtima wapambali: Munthu wopsa mtima msanga.
Chitsanzo: Akutsira mphepotu, ali ndi mtima wapambali.
Mtima wasafuliya: Munthu wosachedwa kupsa mtima.
Amanena zimenezi chifukwa safuliya sachedwa kutentha.
Chitsanzo: Amayi awo ali ndi mtima wasafuliya.
Mtima wokhala pakhundu: Kukhala wopsa mtima msan-
ga.
Chitsanzo: Ali ndi mtima wokhala pakhudu.
Mtimam’malo: Usadandaule.
Chitsanzo: Mtimam’malo, sangakulande ine ndili pompa-
no.
269