Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 27
Paphata pa Chichewa
Chaphazi: Ndalama zomwe umapereka kuti munthu
akakufunire mankhwala kapena ukamutuma
kwinakwake.
Chitsanzo: Ngati mukufuna ndipite kukakusakirani
mtera, ndipatseni chaphazi.
Chatha m’thumba: Wolemera.
Chitsanzo: Bambo amene aja ndi chatha m’thumba,
akhoza kutithandiza.
Chathunthu: Chonse.
Chitsanzo: Ndikufuna chimanga chathunthu osati
chothyola.
Checheta: Kudya momveka phokoso.
Chitsanzo: (1) Akuchecheta makaka kuseriko. (2) Chiswe
chachecheta matabwa onse.
Cheka: Kuthawa.
Chitsanzo: Ataona kuti kwavuta anandiuza kuti, “Cheka!”
Chengetera: Samalira.
Chitsanzo: (1) Muzimuchengetera bwino mwamunayu
angakuthaweni. (2) Mkaziyutu amakuchengeterani.
Chenjera katalumwa: Kuzindikira pambuyo poti
wapusitsidwa kale.
Chitsanzo: Akanadziwa sakanamuthandiza. Wachenjera
atalumwa.
Chenjeza champhongo: Kunyoza kapena kuchitira
chipongwe munthu amene amakuthandiza.
Chitsanzo: (1) Angandichitire chipongwe chotere?
Wachenjeza champhongo, sindidzamuthandizanso. (2)
Wachenjeza champhongo, akadzabweranso adzaona
kokagona.
26