Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 269
Paphata pa Chichewa
(2) Akazi awo amawachitira kamkomya. Nthawi zina
amawaphikira mapawo komanso mtenthandevu.
Mtera: Mankhwala makamaka azitsamba.
Chitsanzo: Asing’anga andipatsa mtera.
Mthenga:
(a) Ubweya wankhukhu.
Chitsanzo: Mphungu sitaya nthenga zake.
(b) Munthu wokapereka uthenga.
Chitsanzo: Sanabwere, koma atumiza mthenga.
Mthirakuwiri: Munthu wabodza yemwe amati akamva
nkhani uku, amaitenga n’kukaikhuthura kwina.
Chitsanzo: (1) Ndinadzidzimuka nditazindikira kuti amayi
amvano aja ndi a nthirakuwiri. (2) Adzakhumudwa
akadzazindikira kuti anzawo aja ndi a mthirakuwiri.
Mthirakuwiri: Munthu wodanitsa.
Chitsanzo: Pamudzi pano pachuluka a mthirakuwiri.
Mthyothyo: Kulira kwa kuthyoka kwa timitengo.
Chitsanzo: Ndinamvera mthyothyo kuti akubwera.
Mtima phaphapha:
(a) Kufunitsitsa utamva zinazake.
Chitsanzo: Ankangoti mtima phaphapha n’kumandi-
yang’ana m’maso.
(b) Kuchita mantha.
Chitsanzo: Nditamva uthengawo mtima wanga umangoti
phaphapha.
Mtima suvala nsanza: Mtima umalakalaka zabwino
zokhazokha.
Chitsanzo: Akuganiza kuti angadzalemere? Zoonadi mtima
suvala nsanza!
Mtima ukhale m’malo: Kuti ndisiye kuda nkhawa.
Chitsanzo: Mpofunika andiuze zotsatira za magazi anga
kuti mtima wanga ukhale m’malo.
268