Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 267
Paphata pa Chichewa
Msampha:
(a) Chinthu chomwe wina amatchera kuti agwire
chiachake. Ingakhale nyama kapena munthu.
Chitsanzo: (1) Akufuna kukutcherani msampha. (2) Wag-
wira mbalame pamsampha.
(b) Zimene munthu amanena kapena kuchita kuti
alowetse wina m’mavuto.
Chitsanzo: (1) Ndinadziwa kuti akunditchera msampha.
(2) Ndalama amandipatsa ija inali msampha.
Msangwe: Kagulu ka nyenyezi zisanu zowala bwino.
Chitsanzo: Kodi unaonapo nyenyezi za msangwe?
Msipu uli kukamwa: Kumwalira akubereka.
Chitsanzo: Akazi awo amwalira msipu uli kukamwa.
Msipu wamera m’khola: Mwayi wopezeka pafupi.
Chitsanzo: Koma apa ndiye msipu watimerera m’khola.
Msonkhano wa mnzanga alipati: Msonkhano waukulu,
wa anthu ambiri.
Chitsanzo: Kwa amfumu kunali chimsonkano cha
mnzanga ali pati.
Msonkhano wa mundipondera mwana: Msonkhano
waukulu, msonkhano wa anthu ambiri.
Chitsanzo: Atsogoleri a chipanichi amanena kuti kudzaka-
la msonkhano wa mundipondera mwana.
Msonkhano wandiweyani: Msonkhano waukulu moti
sungadziwe onse omwe apezekapo.
Chitsanzo: Kuno kuchitika chimsonkhano chandiweyani.
Mswachi: Cheyo chotsukira mkamwa.
Chitsanzo: Andibera nswachi wanga.
Mtanthapalumo: Mawu onena za munthu waukamber-
embere.
Chitsanzo: Ali kuti mtanthapalumo uja?
266