Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 266

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: Ntchitoyi sifuna mphwephwa. (b) Mbewu zopanda kanthu mkati monga mtedza kapena nandolo. Chitsanzo: Andigulitsa mphwephwa zokhazokha. Mpira wamtchemberambayi: Mpira wa azimayi kapena atsikana, mpira wamanja. Chitsanzo: Mfumukazi yanena kuti ithandiza anthu omwe amasewera mpira wamtchemberambayi. Mpishupishu: Kuvutitsa. Chitsanzo: Akungofuna kundipatsa mpishupishu. Mpita: Njira yodutsa nyama zakutchire kapena mbewa. Angatanthauzenso njira yodutsa anthu. Chitsanzo: Ukamafuna kupha mbewa ndi diwa, umafu- nika kutchera pampita. Mpondamakwacha: Munthu wolemera. Chitsanzo: Achimwene awo ndi mpondamakwacha. Mpondamatambala: Munthu wolemera. Kale ndalama za- matambala zidakali zamphamvu, akamatchula munthu wolemera ankamuti mpondamatambala. Chitsanzo: Achimwene awo ndi mpondamatambala. Mpondangolo: Wosabereka. Chitsanzo: Bamboyu ndi mpondangolo. Mpotamanja: Chintchito chachikulu, ndewu kapena nkhondo yaikulu. Chitsanzo: Ntchito imeneyi ndi mpotamanja. Mpsimpsi: Kubwezera chipongwe. Chitsanzo: Mwanayu akuchita mpsimpsi. Mpungwepungwe: Chisokonezo. Chitsanzo: (1) Osamapanga mpungwepungwe angakumangeni. (2) M’tauni muli mpungwepungwe. Mpwechepweche: Zambirimbiri. Chitsanzo: Kwathu zakudya ndi mpwechepweche. 265