Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 264
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: Tikakumane pamphambano.
Mphangala: Munthu wamphamvu komanso wodziwika,
munthu yemwe ambiri amamuopa.
Chitsanzo: Amene uja ndi mphangala.
Mphasa yopinda nthawi yaitali: Munthu wopanda
chikondi.
Chitsanzo: M’nyumba mukakhala mphasa yopinda nthawi
yaitali, umangokhalira kupirira podikirira tsiku loti
udzafe.
Mphasa yoyalula tsiku ndi tsiku: Munthu wokoma mti-
ma.
Chitsanzo: Anthu amenewa akadavutika koopsa, zika-
nakhala kuti alibe mphasa yoyalula tsiku ndi tsiku.
Mphekesera: Nkhani yosatsimikizika imene anthu ambiri
akuikamba mwachinsinsi, nkhani zimene ena amanena
zomwe zilibe umboni weniweni.
Chitsanzo: (1) Mphekesera zikunena kuti watisiya. (2)
Mphekesera zomwe zikumveka ndi zoti bamboyu anakwa-
tirapo.
Mphemvumdyerakumthiko: (1) Munthu wosauka kwam-
biri.
Chitsanzo: Safuna kudzakwatiwa ndi mphemvumdyera-
kumthiko. (2) Popeza ndine mphemvumdyerakumthiko,
ndimangotola zimene atayazo.
Mphepo: Matenda a nthomba.
Chitsanzo: Ndikuopa kupita kumudzi chifukwa kuli
mphepo.
Mpherakuleza: Munthu wachinyengo yemwe
amanamizira kukuchitira zabwino akufuna kukupusitsa,
munthu woonetsa ubwenzi waukulu n’cholinga choti aku-
bere..
Chitsanzo: Chikondi akukusonyezanichi ndi
chachiphamaso, amene uja ndi mpherakuleza.
263