Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 263
Paphata pa Chichewa
Moyo wolowerera: Kukhala ndi khalidwe loipa, kuchita
chiwerewere.
Chitsanzo: Mwana wawo uja anayamba moyo wolowerera.
Moyo wopanikizika: Moyo wovutika.
Chitsanzo: Ndikukhala moyo wopanikizika.
Moyo wopsinyika (wophinjika): Moyo wovutika.
Chitsanzo: Ndikukhala moyo wopsinyika.
Moyo wotayirira: Mawuwa amanena munthu amene
alibe khalidwe labwino, munthu wakhalidwe
lachiwerewere.
Chitsanzo: Amakhala moyo wotayirira.
Moyo wovuta: Moyo wovutika kwambiri.
Chitsanzo: Ku Malawi kuno kuli moyo wovuta.
Mpalu: Mlenje.
Chitsanzo: Nimurodi anali mpalu woopsa.
Mpamba: Ndalama zoyambira bizinezi. Mawuwa angatan-
thauzenso zinthu zimene umadalira.
Chitsanzo: (1) Moyo ndi mpamba. (2) Ndikhoza kuyamba
bizinezi nditapeza mpamba.
Mpando wonona: Udindo wabwino, waukulu.
Chitsanzo: Analowa m’chipembedzochi chifukwa
ankafuna mpando wonona.
Mpando wonona: Udindo wobweretsa ndalama zambiri.
Chitsanzo: Mipando yonse yonona anapatsa abale awo.
Mphambano:
(a) Nthawi yoti usankhe chimodzi. Pamphambano ndi ma-
lo amene pagawanika njira. Munthu sungadutse njira
zonse nthawi imodzi, umafunika kusankha yoti udutse.
N’chimodzimodzinso ukakula, umafunika kusankha zin-
thu zina pamoyo wako ufune usafune.
Chitsanzo: Moyo wanga wafika pamphambano.
(b) Malo omwe pakumana kapena kusiya misewu.
262