Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 262
Paphata pa Chichewa
(b) Amanenedwanso ngati munthu akunena kuti kulibe
zamasewera.
Chitsanzo: Lero kuli motomoto.
Mowa uli m’mutu: Ataledzera.
Chitsanzo: N’chibwana kumayendetsa galimoto mowa uli
m’mutu.
Moyo kuonera pakhosi: Munthu amene wangotsala
pang’ono kufa moti mukudziwa zoti ali moyo poona kuti
pakhosi pakutukula.
Chitsanzo: Adwala kwambiri moti moyo tikungoonera
pakhosipa.
Moyo ukupereseka: Kudwala mwakayakaya, moyo
ukutha.
Chitsanzo: Anabwera kudzationa moyo wa amayi
ukupereseka.
Moyo wamphale: Moyo wabwino komanso wopanda
mavuto.
Chitsanzo: “Muli bwanji anzathu?” “Ayi, ife moyo wathu
ndi wamphale.”
Moyo wamthombozi: Moyo woti pena ziyenda pena
sizikuyenda. Nthombozi ndi mtengo womwe umakhala
kwina kouma kwina kwakuwisi.
Chitsanzo: Ife ndiye bola tikupuma, moyo wathu ndi
wamthombozi.
Moyo wankhumba: Moyo woyenda kwinaku ukubuula.
Chitsanzo: Mmene zinthu zavutiramu, moyo wa anthu
ambiri ndi wankhumba.
Moyo wawofuwofu: Moyo wofewa.
Chitsanzo: Anazolowera moyo wawofuwofu.
Moyo wofewa: Moyo wabwino kwambiri.
Chitsanzo: Anazolowera moyo wofewa.
261