Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 260
Paphata pa Chichewa
Mnzanga wa ponda apa mpondepo: Mnzanga wapam-
tima, mnzanga amene ndimayenda naye kulikonse.
Chitsanzo: Amene uja ndi mnzanga wa ponda apa
mpondepo.
Mnzanga wabere: Mkazi mnzanga.
Chitsanzo: Sindingachite manyazi ndi mnzanga wabere.
Mnzati: Munthu wolimba, wothandiza pamavuto, mtengo
womwe umachirikiza tsindwi kuti lisalowe mkati.
Chitsanzo: (1) Amenewa ndi mnzati pabanjali. (2)
Ukachotsa mnzatiwu, dengali liloshoka.
Modzitukumula: Monyada, modziyesa wapamwamba,
kudzimva.
Chitsanzo: Dzulodzuloli amadutsa akuyenda modzituku-
mula.
Molalo:
(a) Kuchemerera.
Chitsanzo: Masapota a timu iyi ali ndi molalo.
(b) Kukopa mitima ya anthu.
Chitsanzo: Munthuyu ali ndi molalo.
Monyanyira: Mopitiriza muyezo, mosadzilemekeza.
Chitsanzo: (1) Mayiwa amachita zinthu monyanyira. (2)
Atsikanawa avala monyanyira.
Mopanda dongosolo: Mwachisawawa, mosalongosoka.
Chitsanzo: Sindimafuna kuti anthu amene
ndikuwayang’anira azichita zinthu mopanda dongosolo.
Mosadzilemekeza: Mosadzipatsa ulemu, kuchita zinthu
zosayenera, kuchita zinthu ngati mwana.
Chitsanzo: Avala mosadzilemekeza.
Mosadzimanga: Momasuka.
Chitsanzo: Nena mosadzimanga ngati umandikondadi.
Mosalongosoka: Mopanda dongosolo.
Chitsanzo: Sindimafuna kuti anthu amene
259