Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 259
Paphata pa Chichewa
Mlezi: Munthu yemwe amalera mwana wamng’ono mpaka
atakula. Nthawi zambiri amakhala wantchito.
Chitsanzo: Uyu ndi mlezi wa mwanayu.
Mliyenda: Moyenda.
Chitsanzo: Akulu anu ali mliyenda.
Mlongoti: Mtengo woongoka, pholo.
Chitsanzo: Amusenzetsa mlongoti.
Mluzu wa galu ndi umodzi: Aliyense amene wamva
kuitana asayembekezerenso uthenga wina azingobwera.
Chitsanzo: Aliyense akamva kuitana azingobwera, pajatu
mluzu wa galu ndi umodzi.
Mmangummangu: Mofulumira.
Chitsanzo: Tiyeni tizichita zinthu mmangummangu,
angatipeze pompano.
Mmemo: Nsima yophikidwa pogwira ntchito. Nthawi zam-
biri siphikidwa kapena kupakulidwa mwadongosolo.
Chitsanzo: Ntchito zolimba ngati izi zimafuna mmemo.
Mnefiri: Munthu wamphamvu, wogwetsa, wandewu.
Chitsanzo: (1) Mwanayutu akulimbana ndi Anefiri. (2)
Amene uja ndi Mnefiri.
Mnjunju: Munthu wosamva za ena kapena waliuma.
Chitsanzo: Umachedwa kwambiri ukakumana ndi
wapolisi wamnjunju pamalo ochitira chipikisheni.
Mnkhang’a: Munthu wokakamira.
Chitsanzo: Amene uja ndi mnkhang’a, akakumatirira sa-
kusiya.
Mnyezi: Manyazi.
Chitsanzo: Atamugwira akuvuula ndiwo mumphika,
anayamba kuchita mnyezi.
Mnzanga wa pabondo: Munthu amene umakondana naye
kwambiri kuyambira kale.
Chitsanzo: Ameneyu ndi mnzanga wa pabondo, tinadziwa-
na kale kwambiri.
258