Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 258

Paphata pa Chichewa (b) Kusafuna kuchoka pamalo. Chitsanzo: Anthu ambiri amachita mkondwa akapita ku Jubeki chifukwa choopa kuchita manyazi kuti anthu awaseka akabwerako chimanjamanja. Mkuntho: (a) Kumenya. Chitsanzo: Njoka simafa ndi mkuntho umodzi. (b) Mvula ikamagwa mwamphamvu komanso ndi mphepo timati ikugwa mwankuntho. Chitsanzo: Dzulo kunagwa chimvula chankuntho. Mkupamame: Munthu yemwe umapita naye kokafunsira. Chitsanzo: Ukukumbukira muja ndinabwera kwanu ndi mkupamame. Mkute: (a) Chakudya chomwe chagona, chomwe chinaphikidwa dzulo. Chitsanzo: Musandiwerengere phalalo, ine ndidya mkute. (b) Nkhani kapena ntchito yadzulo. Chitsanzo: Dzulo tinasungira mkute, tiyeni timalizitse kaye zimenezo kuti tiyambe za lero. Mkuzi: Chingwe chomangira buluku kapena siketi kuti isagwe. Chitsanzo: Njatani bulukulo ndi mkuzi. Mleme: Munthu yemwe samaona bwino. Chitsanzo: Amene uja ndi mleme, maso ake anatha kalekale. Mlerakhungwa: Munthu wothandiza kwambiri. Chitsanzo: Tabwera kwa inu chifukwa tikudziwa kuti ndinu mlerakhungwa. Mlesi: Munthu wosakonda kugwira ntchito. Chitsanzo: Anakwatira mlesi. 257