Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 255

Paphata pa Chichewa (b) Menya kwambiri. Chitsanzo: Mwana wojaira amafunika kumuminitsa. Minyama: Tsoka. Chitsanzo: Anthu inu ndi amene mukundipatsa minyama. Miphika siphulana: Amene ali m’mavuto okhaokha san- gathandizane. Chitsanzo: Zativuta tonse, miphika siphulana. Mira pachipande: Nama. Chitsanzo: Ndinkadziwa ine kuti akumira pachipande. Misozi ikumuyabwa: Ukufuna kulira. Chitsanzo: (1) Ngati misonzi ikukuyabwa, bwanji osaiphinya? (2) Azimayi ambiri misozi ikamawayabwa, amayamba kuputa amuna awo. Akawamenya amalira mo- satonthozeka ndipo akamaliza kulirako, amauza amuna awowo kuti, “Mukufuna ndikakuikireni madzi osamba?” Misozi ya Farao: Kachaso. Chitsanzo: (1) Anthu amene amamwa misozi ya Farao amaderera mitundu ina ya mowa. (2) Atamupeza atauma ali gwa. Zikuoneka kuti anamwalira atamwa mutu wa misozi ya farao osadyera. Misozi yalengeza: Misozi yayamba kuonekera m’maso. Chitsanzo: Atangomutsina, misozi inalengeza m’maso. Mitala: Kukwatira mkazi wina uli kale ndi mkazi wina, kukhala ndi akazi angapo. Chitsanzo: Bambo wolumala aja anakwatira mitala. Mithulo: Womana. Chitsanzo: Mwanayu ndi wamithulo. Mitsamiro: Wopita naye kumanda. Chitsanzo: Ena akatenga kachilombo, amakafalitsa kuti akhale ndi mitsamiro yambiri. Mituka: Katundu makamaka chakudya chomwe umatenga paulendo, pokaona athu. 254