Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 254

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: Mwanayu ndi wamiliri. Mimba ngati dzenje lopanda malire: Wokudya kwambiri. Chitsanzo: Ali ndi mimba yangati dzenje lopanda malire, moti inenso ndimadabwa kuti chakudya chonsechi chimalowa m’thupi mwakemu? Mimba tiyetiye: Munthu wokonda kudya koma ntchito ayi. Mawuwa amathanso kugwiritsidwa ntchito ponena monyoza munthu yemwe akungotsatira anthu koma asa- kufunidwa. Chitsanzo: Tawaonerani, ikakwana 12 koloko ndiye mim- ba tiyetiye, kumabwera kuno kuti adzaipeze itapsa. Mimba yakhonde: Munthu wa mimba yaikulu. Chitsanzo: Anthu ambiri olemera amakhala ndi mimba zakhonde. Mimba: Kuyembekezera mwana, kukhala ndi pathupi. Chitsanzo: Mtsikana uja ali ndi mimba. Mimbulu: Anthu olusa, anthu ovuta. Chitsanzo: Sindingamakhale ndi mimbulu ili pakhomo pa- noyi. Mina: Khaula. Chitsanzo: Ndachimina, sindidzapitanso kumene kuja. Minga umabwera ndi mafinya omwe: Pali zovuta palinso zokoma. Chitsanzo: Kulima n’kopweteka, komabe osasiya kulima chifukwa munga umadza ndi mafinya omwe. Mingoli: Nyimbo, mawu okometsera poyimba. Chitsanzo: (1) Amakonda kumvetsera mingoli. (2) Mingoli ya nyimboyi ndi yosangalatsa. Minitsa: (a) Lapitsa. Chitsanzo: (1) Anasiya kuvuta atawaminitsa. (2) Achimina kuti sadzapitakonso. (3) Anthu akhalidwe lotere amafunika kuwaminitsa. 253