Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 253

Paphata pa Chichewa Mgonero: Chakudya chamadzulo. Chitsanzo: Ndinawapeza akudya mgonero. Mgugu: Phokoso la mapazi kapena la kugogoda. Chitsanzo: Kodi mgugu ukumveka kuseriwo ndi wa chiyani? Mgula: Mzere wa kumapeto kwa munda kapena m’malire a malo. Nthawi zambiri umakhala waukulu kwambiri. Chitsanzo: Tilime mgula apa kuti madzi asaphwasule. Mgwidyo: Phokoso la madzi kapena zakumwa zina ukam- ameza. Chitsanzo: (1) M’kapumutu mwangotsala migwidyo iwiri! (2) Akamamwa madzi amamveka migwidyo. Michokocho: Anthu olongolola. Chitsanzo: Kodi michokocho inali kuseri ija yachoka? Midenga: Mitsuko. Chitsanzo: Anyamula midenga akulowera kunsika. Migolomigolo: Zambirimbiri. Chitsanzo: Amamwaza ndalama ngati ali nazo migolomigo- lo. Mikokoyogona: Akuluakulu apamudzi. Chitsanzo: Zimene achitazi zaimitsa mitu mikokoyogona. Mikwingwirima: Mavuto osaneneka, khaulitsa. Chitsanzo: Akukumana ndi mikwingwirima yambiri. (2) Atapita kutauni anakumana ndi mikwingwirima. Milandu siwola: Ukapalamula, mlanduwo umakhalapobe mpaka utatha. Chitsanzo: Ankaganiza kuti akathawa tiiwala, mlandutu suwola! Miliri: (a) Matenda omwe amafala mofulumira kwambiri. Chitsanzo: Masiku ano miliri yangoti mbwee. (b) Kumana, kuumira. 252