Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 252
Paphata pa Chichewa
Meta: Chenjeretsa, kupusitsa.
Chitsanzo: Amalonda a masiku ano cholinga chawo
chimakhala kumeta anthu kuti apindule.
Mezera mate: Osanena kanthu.
Chitsanzo: Nkhani zina zimangofunika kumezera mate.
Mfana: Mwana.
Chitsanzo: (1) Usamachite makani mfana. (2) Mafana am-
biri akumachita mano.
Mfumu: Mtembo kapena thupi la munthu wakufa.
Chitsanzo: (1) Anyakwawa anauza onse kuti aimirire
n’cholinga choti atulutse mfumu kuchokera m’nyumba. (2)
Amene atapezeke atakhala pansi tikamatulutsa mfumu
yathu m’nyumbamu, alipira chindapusa.
Mfundo zawedewede: Mfundo zosathandiza, mfundo
zosagwira mtima.
Chitsanzo: Mfundo zimene amanena ndi zawedewede.
Mfundu: Zinthu zimene zimabwera m’mutu khukhu
lam’mutu likathetheka.
Chitsanzo: M’mutu mwake mumachoka mfundu
akamapesa.
Mfupidoli: Munthu wamfupi.
Chitsanzo: Munthu akakhala mfupidoli, amavutika
kutenga zinthu zomwe zili pamwamba.
Mfwisuro: Chakudya cha m’mawa.
Chitsanzo: (1) Bwerani kuno mufwisure. (2) Tiyeni tikadye
mfwisuro.
Mgodi:
(a) Malo amene munthu amapezako ndalama.
Chitsanzo: Umenewu ndi mgodi wanga.
(b) Kuchimake.
Chitsanzo: Kumeneku ndi kumgodi kwa ndalama.
( c) Phanga
Chitsanzo: Anthu onse analowa kumgodi.
251