Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 250

Paphata pa Chichewa Chitsanzo: Akamayerekedwa azikumbukira kuti chuma ndi m’chira wa khoswe. Mdadada: Nyumba zolumikizana. Chitsanzo: Mdadada wonsewu chimbudzi ndi chimodzi. Mdala: Mawu onyoza ponena za bambo. Chitsanzo: Mdalayu ndi khuluku. Mdidi: (a) Matenda otuluka thumbo. Chitsanzo: Akudwala matenda a mdidi. (b) Kamvekedwe kamapazi poyenda, kugunda. Chitsanzo: Ndinamva mdidi kuseriku, kodi pali amene anatuluka panja? Mdima usaka: Pa nthawi yamasana munthu umachenjera, koma madzulo umasowa kolowera. Chitsanzo: Si wathawa, musiyeni, mdima umusaka. Mdima wa ndiweyani: Mdima waukulu. Chitsanzo: Magetsi atazima, mnyumbamo munali mdima wa ndiweyani. Mdima wa tsokomola ndingakuponde: Mdima waukulu. Chitsanzo: Mphangalo munali m’dima wa tsokomola ndingakuponde moti tinkafunika kunyamula miuni. Mdima: Maliro. Chitsanzo: Anatithandia kwambiri mdima utatigwera pakhomo pano. Mdukamanja: Woduka manja. Chitsanzo: Kodi mdukamanja uja ali kuti? Mdyerekezi: Munthu woipa kwambiri. Limenelinso ndi dzina limene mngelo woipa anavala atagalukira Mulungu m’munda wa Edeni. Chitsanzo: Iwe ndiye ndi mdyerekezi ndithu, sumupha mnzako? 249