Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 25

Paphata pa Chichewa Chalaka bakha: Chakanika wamkulu mwana sangachithe, chakanika katswiri ndiye kuti munthu chisawawa sangachithe. Chitsanzo: Ngati chalaka bakha ndiye nkhuku ngati iwe ungatani? Cham’kuka: Munthu wokonda kukhala pamodzi ndi akazi. Chitsanzo: (1) Amene uja ndi cham’kuka. (2) Athamangitseni a cham’kukawa. Chamba: (a) Kupusa, munthu wosokonekera. Chitsanzo: Inetu sindifuna munthu wachamba. (b) Mtundu wa nyimbo (gule). Chitsanzo: Amaimba chamba cha Beni. (c) Fodya wamkulu. Chitsanzo: Anavula pansika atasuta chamba. Chamlomo: Amenewa ndi malipiro amene munthu amapatsidwa chifukwa choyankhula. Mwachitsanzo pokafunsira mbeta nthawi zambiri okafunsirawo amapereka chiwongo kapena chansana kwa makolo a mkaziyo. Koma kwa munthu amene anayankhula pokafunsirapo, amamupatsa chamlomo. Chitsanzo: Tantha mpweya wathu pokulankhulirani kumene kuja, nafenso tipatseni chamlomo. Chamseri: (a) Chakumbali osati pagulu. Chitsanzo: Akuchita chibwenzi chamseri. (b) Kuchita zinthu mwachinsinsi. Chitsanzo: Tiyeni tikumane chamseri. 24