Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 248

Paphata pa Chichewa (c) Apolisi. Chitsanzo: (1) Amindibasi akuthawa mbola. (2) Kutsogoloku kuli mbola. Mbombo: Munthu womana. Chitsanzo: Ali kuti mbombo uja? (2) Mwanayu ndi mbom- bo. Mbonaona: Mavuto kapena zosautsa. Chitsanzo: Atamugwira akukhonyola chimanga m’munda wa eni, anyamata a pamudzipo anamuonetsa mbonaona. Mbonga: Mpala wotheratu. Chitsanzo: (1) Anthu ambiri akamachokera kujoni amabwera atameta mbonga. (2) Ulendo uno ndimetetsa mbonga. Mbota: Nsambo, angatanthauzenso zingwe. Chitsanzo: Ndi katswiri pankhani yokanyanga mbota. Mbulanda: Ali wosavala, munthu wosavala kalikonse. Chitsanzo: (1) Mmene anthu akuvalira masiku ano n’chimodzimodzi kuyenda mbulanda. (2) Chamuchitikira n’chiyani kuti azingoyenda mbulanda. Mbuliuli: Chimanga chophulika. Chitsanzo: Chimanga chimene wakazinga chili mbuliuli zo- khazokha. Mbuto: Malo amene munthu amakhala. Chitsanzo: Mbuto yawo ndi imeneyi. Mbutuma: Munthu wopusa. Chitsanzo: (1) Akatsegula pakamwa m’pamene umadziwa kuti ndi chimbutuma. (2) Anangoona kukula, ndi mbutuma. Mbuzi ikakondwa, amalonda ali pafupi: Munthu ukamavuta ndiye kuti watsala pang’ono kulira. Chitsanzo: Ndinadziwa ine, kuthamangathamanga kwake 247