Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 247

Paphata pa Chichewa Mbambande: Chinthu chabwino kwambiri. Chitsanzo: (1) Malaya amene ndagula ndi mbambande. (2) Mwana amene uja ndi mbambande. Mbanda: Chifwamba. Chitsanzo: Umbanda ukuchuluka m’tauni muno. Mbava: Munthu wakuba kapena mbala. Chitsanzo: Mudzasiya chibwana chimenechi mukadzakumana ndi mbava. Mbawalagomo: Nyani. Mawu onena mwachining’a omwe ena amagwiritsa ntchito ponena za nyani. Amagwiritsa ntchito mawu amenewa akamafuna kumupanga ndiwo. Nanga aipe ndi dzina lomwe, bola kumupatsa lodyera. Chitsanzo: Lero aphika mbawalagomo. Mbewu zacha (zipatso zacha): Zakhwima, zayamba kup- sa. Chitsanzo: (1) Chimanga chacha. (2) Mbewu zikayamba kucha, anthu amanenepa. Mbiya: Munthu amene sadziwa kusambira. Chitsanzo: Enafe ndi mbiya, kugwera m’madzi timangopi- ta pansi ngati mwala. Mbiyang’ambe: Chidakwa, chiledzerere, munthu wosachoka pamowa. Chitsanzo: Ngati ukufuna kuona mbiyang’ambe zenizeni, pita kwa Mayi Mbiyazapolama. Mbola: (a) Mbola ndi kanthu kokhala ngati minga koma kamatsala pathupi njuchi kapena mavu akakuluma. Chitsanzo: Njuchi ikaluma imasiya mbola. (b) Makani. Chitsanzo: Musiyeni, akakumana ndi anzake amuchotsa mbola. 246