Agoloso Presents - Atondido Stories Agoloso Presents - Paphata pa Chichewa | Page 245
Paphata pa Chichewa
Chitsanzo: Ndimayesa atsala olongosoka ndi amenewatu,
ndiye ayambanso kuba. Ayi ndithu, mavuto si maliro okha!
Mavuvu: Kuvuta, kuchita zinthu mwaphuma.
Chitsanzo: (1) Mayiyu ndi wa mavuvu. (2) Munthuyu
amachita zinthu mwamavuvu.
Mawaya anaduka: Saganiza bwino.
Chitsanzo: Achimwene anuwa m’mutumu mumakhala
ngati mawaya ena anaduka.
Mawere awirirana: Kudana kwa pachibale.
Chitsanzo: (1) Osamalowerera mawere akawirirana. (2)
Ndinapeza pakhomopo pali pokopoko, zikuoneka kuti
mawere awirirana.
Mwana wapabondo: Mwana wokondedwa.
Chitsanzo: Ameneyu ndiye mwana wawo wapabondo.
Mawu adakali m’kamwa: Adakayankhula.
Chitsanzo: Mawu adakali m’kamwa, anangoona watulu-
kira.
Mawu apatali: Mawu ozama.
Chitsanzo: M’nkhaniyi mwachuluka mawu apatali.
Mawu okhadzula: Mawu opweteka komanso amwano.
Chitsanzo: Amakonda kuyankhula mawu okhadzula. Uka-
wafunsa amanena kuti ndi mmene alili tingowazolowera.
Mawu olasa mtima: Mawu opweteka, okhumudwitsa.
Chitsanzo: Anandiyankha mawu olasa mtima.
Mawu oumitsa pakamwa: Mawu ovuta kuwatchula,
mawu otukwana.
Chitsanzo: Sindingayerekeze kutchula mawu oumitsa
pakamwawo.
Mayi akunyumba: Mawu amenewa amanenedwa ndi
mwamuna akamauza ena za mkazi wake. Koma azimayi
ambiri amadana ndi zoti mwamuna wawo aziwanena kuti
244